Get all 36 Songs for Saplings releases available on Bandcamp and save 35%.
Includes unlimited streaming via the free Bandcamp app, plus high-quality downloads of Songbook for the Soul, Volume 1, أسئلة واجابات كلمات الالبوم الثانى : السقوط والخلاص, Запитання та відповіді том 6: Христос і Його повернення (Ukrainian), Mafunso Ndi Mayankho Vol. 3: Khristu Ndi Ntchito Zake (Chichewa), Mafunso Ndi Mayankho Vol. 4: Mau A Mulungu (Chichewa), Запитання та відповіді том 5: Молитва і таїнства (Ukrainian), Запитання та відповіді том 4: Слово Боже (Ukrainian), Запитання та відповіді том 3: Христос і Його діяння (Ukrainian), and 28 more.
1. |
MLUNGU NDI NDANI?
01:59
|
|||
1. MLUNGU NDI NDANI?
Mlungu ndi ndani?
Mlungu ali yekhayo, wamoyo oona
Ndiwaulemerero, wamphamvu amadziwa
zonse,
Namalenga wamkulu, ndi mbuye, wadziko—lonse
Mulungu wabwino, oyera, osatha—wamuyaya, osasintha
Mulungu ndi ndani?
Osatha wamuyaya
Mulungu wamuyaya wabwino, oyera, osatha osasintha.
sitingamvetse ulemerero wa Mulungu
Wamuyaya osasintha, wosaoneka, Mulungu yekhayo kukhale ulemu, kunthawi zonse.
(1 Timothy 1 ndime 17)
Kukhale ulemu, kunthawi zosatha Amen
|
||||
2. |
ANALENGA MULUNGU NDANI?
00:58
|
|||
2. ANALENGA MULUNGU NDANI?
Analenga Mlungu ndani?
Analenga Mlungu ndani?
Palibe anamulenga
Palibe anamulenga
Chorus
Asanabadwe mapiri
Musanalenge dzikoli
Nthawi yosayamba mpaka yosatha
Ndinu Mulungu
(Masalimo 90 ndime 2)
|
||||
3. |
||||
3. KODI MULUNGU ALI NDI CHIYAMBI?
Kodi Mulungu ali ndi chiyambi?
Ayi Mulungu ndi wamuyaya
Woyera woyera Ambuye
Amene analipo, alipo, adzakhalapo
Woyera woyera ,ndi Ambuye
Mulungu wamphamvu
Analipo alipo adzakhalapo
(Chivumbulutso 4 ndime 8)
|
||||
4. |
||||
4. KODI MULUNGU ANGATHE KUFA?
Kodi Mulungu angathe kufa?
Ayi ndi wamuyaya
Chorus 1
Kunthawi zanthawi zanthawi zamuyaya
Ndi Mlungu wamoyo ndi mfumu yamuyaya
(yeremiya 10; 10)
Chorus 2
Zaka zanu zikhalira mibadwo mibadwo
Zaka zanu sizifikira kuthaaaa
(Masalimo 102 ndime 24 ndi ndime 27)
|
||||
5. |
||||
5. KODI KULINSO MULUNGU WINA?
Kodi kuli Mulungu wina?
Ayi woona ndi m’modzi
Kodi kuli Mulungu wina
Mulungu ndi m’modzi yekha
Pa Yesaya 45 Mulungu ati
Ine ndine Yehova, popanda Ine palibe Mulungu
Ine ndine Mulungu, palibenso wofananane
Ine ndine Mulungu palibenso
Palibe Mlungu opanda Ine
Idzani kwa Ine mupulumuke
Nonse padziko pakuti
Ndine Mulungu
Wolungama ndi mpulumutsi
Idzani kwaine mupulumuke
Nonse padziko poti
Ndine Mulungu
|
||||
6. |
||||
6. MULUNGU M’MODZI APEZEKA KANGATI?
Mulungu m’modzi apezeka kangati?
Mlungu m’modzi mwa atatu
Mulungu m’modzi apezeka kangati?
Mlungu m’modzi mwa atatu
Chisomo cha Ambuye, Yesu Khristu, Chikondi cha Mulungu ndi Chiyanjano cha Mzimu Woyera chikhale ndi inu nonse
2 Akorinto 13 ndime 14
Chisomo cha mbuye Chikhale nanu
|
||||
7. |
||||
7. MULUNGU MWA ATATU NDI NDANI?
Mulungu mwa atatu ndi ndani?
Mulungu mwatatuyo ndi Atate, Mwana
Mzimu woyera
Mukani phunzitsani anthu onse
Ndi kuwabatiza m’dzina laTate,
Mwana, ndi Mzimu Woyera
(Mateyu 28 ndime 19)
|
||||
8. |
MULUNGU ALI KUTI?
02:31
|
|||
8. MULUNGU ALI KUTI?
Ndingapite kuti kuzemba mzimu wanu
Ndithawire kuti kuzemba kupezeka kwanu
Ndingapite m’mwamba, muliko
Ndingakoze kamalanga, pansi, muliko
Mlungu ali ku?
ponsepo
Mlungu ali ku?
Ponsepo
Mulungu ali ponsepo
Ndingakoze kamalanga pansi, muli konko
(Masalimo 139 ndime 7 ndi 8)
Mulungu ali ponseso.
|
||||
9. |
MUNGAONE MLUNGU?
01:47
|
|||
9. MUNGAONE MLUNGU?
Mungaone Mlungu?
Ayi, Mulungu ndi Mzimu, ndipo alibe
Thupi ngati munthu
Mungaone Mlungu?
Ngakhale sindimuona
Ndidziwa kuti, andiona nthawi zonse
Ndine Mulungu wapafupi ,si Mlungu wa patali
Ndani munthu angabisale, kuti ine
Ndisamuone? Kodi sindidzala kumwamba ndi pansi
Ati Yehova
Yeremiya 23 ndime 23--24
|
||||
10. |
||||
10. KODI MULUNGU ADZIWA ZONSE?
Kodi Mlungu adziwa zonse?
Inde adziwa zonse
Palibe chobisika kwa Iye
Maso ake ali panjira ya aliyense
Napenya moponda mwake
(Jobu 34:21)
Maso a Mulungu ali ponsepo
Ayang’ana abwino ndi oyipa
(Miyambo 15 ndime 3)
|
||||
11. |
||||
11. KODI MULUNGU ANGATHE ZONSE?
Kodi Mulungu angathe zonse?
Inde chifuniro chake choyera
Ndi Mulungu zonse zotheka
Mateyu 19 ndime 26
Kodi Mulungu angathe zonse
Inde chifuniro chake choyera
|
||||
12. |
ANAKULENGA NDANI?
01:19
|
|||
12. ANAKULENGA NDANI?
Anakulenga ndani?
Mulungu
Ndidziwa anandilenga
Pa Genesisi 1 ndime 27 Mau a Mulungu ati
Analenga munthu mchifanizo chake
Mchifanizo chake Mulungu
Analenga mwamuna ndi mkazi
Anakulenga ndani?
Ndidziwa anandilenga
|
||||
13. |
ANAKULENGERANJI MULUNGU?
02:40
|
|||
13. ANAKULENGERANJI MULUNGU?
Anakulengeranji Mlungu?
Anakulengeranji Mlungu?
Kodi udziwa?
Anandilenga ndizimulemekeza
Ndikukondwera naye nthawi zonse
Chorus
Mungakhale mudya kapena kumwa
Kaya muchita kanthu kena
Chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu
Chorus
Ndingakhale ndidya kapena kumwa
Kaya ndichita kanthu kena
Ndichite zonse ku ulemerero wa Mulungu
( 1 Akorinto 10 ndime 31)
Anandilenga ndizimulemekeza
|
||||
14. |
||||
14. NDI CHANINSO CHOMWE MULUNGU ANALENGA?
Ndichaninso chomwe
Mulungu analenga?
Mulungu analenga zinthu zonsezi
Chorus
Pachiyambi Mulungu analenga
Kumwamba ndi pansipa
Analenga kuwala usana ndi usiku, thambo ndi Nyanja
Ndi zomera zonse
Kenako chopambana
Analenga munthu
M’chifanizo chake analenga
Mwamuna ndi mkazi
(Genesisi mutu woyamba)
|
||||
15. |
||||
15. MULUNGU ANALENGERANJI ZONSEZI?
Mlungu analenganji zonse?
Ulemerero wake
Chifukwa cha ulemerero wake
Analenga zonsezi
Zonse zichokera kwa Iye
Zichitika kufikira kwa Iye
Ulemerero kunthawi zonse
Aroma 11 ndime 36
KwaIye Ulemerero
Kunthawi zonse Amen.
|
||||
16. |
||||
16. UNGATAMANDE BWANJI MLUNGU?
Ungatamande Bwanji Mlungu?
Ndingatamande po mukonda
Ndikuchita zomwe walamula
Wakuonetsa Munthuwe chifundo
Zabwino ndinso Ambuye afuna kwa iwe
kuchitachilungamo
Ndi kukonda chifundo
Kudzichepetsa ndi Mulungu wako
(Mika 6 ndime 8)
|
||||
17. |
||||
17. CHIFUKWA CHANI NDILEMEKEZE MLUNGU?
Lemekezani Yehova
Amitundu nonse padziko
Chikondi chake n’chachikulu
Kwa ife
(Masalimo 117)
Chifukwa chiani ndilemekeze Mlungu?
Ndizimulemekeza
Chifukwa chiani ndilemekeze Mlungu
anandilenga
Chifukwa chiani ndilemekeze Mlungu
Andisamalira
Ndilemekeze Mlungu wanga
|
||||
18. |
||||
18. MAKOLO ATHU OYAMBA NDANI?
Makolo oyamba ndani?
Adamu ndi Hava
Adamu ndi Hava ndi makolo oyamba
Chorus
Kenako Mulungu anati
Sibwino munthu akhale yekha
Ndimpangira womuthangatira
Ndipo analenga mkazi napita naye kwa mamuna
Anamutcha Hava m’mayi wa anthu onse
(Genesisi 2 ndi 3)
|
||||
19. |
||||
19. MULUNGU ANAWUMBA BWANJI ADAMU NDI HAVA?
Mulungu adawumba bwanji Adamu ndi Hava?
Mulungu anawumba Adamu ndi dothi lapansi,
adawumba bwanji Adamu ndi Hava?
Mulungu anawumba Adamu ndi dothi lapansi,
Napanga Hava ku mthiti ya Adamu
Genesisi 2 ndime 7
anawumba munghu ndi dothi la pansi
Genesisi 2 ndime 22
napanga mkazi ku mthiti ya mamuna
|
||||
20. |
||||
20. ANAPEREKA CHIANI MULUNGU KWA ADAMU NDI HAVA PAMWAMBA PA THUPI?
Anapereka chiani kwa Adamu ndi Hava pamwamba pa thupi?
Mulungu anawapatsa mzimu womwe sudzafa
Anapereka chiani kwa Adamu ndi Hava pamwamba pa thupi?
Mulungu anawapatsa mzimu womwe sudzafa
Ambuye anapanga muthu kuchoker ku dothi lapansi
Nauzira munthuo mpweya wa moyo
Ndipo munthu anakhala wamoyo
Mulungu anamuuzira mpweya wa moyo
Genesisi 2 ndime 7
Mulungu anamuuzira mpweya wa moyo
|
||||
21. |
||||
21. KODI ULI NDI MZIMU NDIPONSO THUPI?
Kodi uli ndi mzimu ndiponso thupi?
Inde mzimu womwe sudzafa
Kodi uli ndi mzimu ndiponso thupi?
Inde mzimu womwe sudzafa
Mlaliki 12 ndime 7
Fumbi ku fumbi
Mzimu kubwerera kwa Mulungu anaupereka
|
||||
22. |
||||
22. KODI ADAMU NDI HAVA MULUNGU ANAWALENGA OTANI?
Kodi Adamu ndi Hava
Mulungu anawalenga otani?
Anawalenga amgwiro ndi okondwa
Genesis 2 ndime 25
Onse anali okondwa
Genesis 2 ndime 25
Anali okondwa opanda manyazi
|
Songs for Saplings Portland, Oregon
We create lively, fun songs that attempt to deliver the deepest Biblical truths in a format that children will
love.
Songs for Saplings is James and Dana Dirksen. We live in Portland, OR, and have 6 beautiful children. We thank God that He has allowed us to share the Good News that Jesus came to seek and save that which was lost.
You can learn more about us at songsforsaplings.com
... more
Streaming and Download help